Chichewa Christian Hymns
Hymn 410 MAWU akewo anamveka ponse,
MAWU akewo anamveka ponse,
Olalikidwa ndi aneneriwo;
Kuti yense wakumvera mawuwo,
Apulumuke.
(Mawuwo) Amveke,
(Tu) Kwa onsewo;
(Wo) Muetseratu ‘we sadzafa ndithu.
Tamveratu ‘we Mawu a Mulungu,
Khulupilira mwa
Ambuye Yesu;
Udzalandira moyo wosathawo,
Udzakondwera.
Tsoka kwa iye wosakhulupira,
Zolalikidwa ndi aneneriwo;
Koma patsiku la chiŵeruziro,
Adzafa ndithu
