Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 39 MUNASIYATU dziko lanulo,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 39 MUNASIYATU dziko lanulo,

 

MUNASIYATU dziko lanulo,
E, chifukwa cha íne;
Ndi ku Betlehemuko,
Pakubadwa Inu,
M’nyumba zawo nakukanani.

Mbuye Yesu, lowani ‘mtima,
Nyumba yanu ndi mtima’nga;
Mbuye Yesu, lowani ‘mtima,
Nyumba yanu ndi mtima’nga.

Akumwambako nayimbitsatu,
Kukulemekezaní;
Koma monga mwana,
M’dziko munabadwa,
Munadzíchepetsadi.

Nyama za mthengo ndi mbalamezo,
Zili namo mogonamo;
Koma Mwana Mlungu,
Analibe nyumba,
M’mapululu nagonatu.

Munadzera ndi mawu amoyo,
Akupulumutsa anthu;
Anakaníza,
Anasautsa,
Anapachika Inu.

Mmene mubwera kutiŵeruza,
Ndi angelo oyimbira;
Mundiitane,
Muti, “Idza ‘we,
Khala nane Kumwamba.”

Mtima wanga udzakondwera,
Mmene mundilandiranso;
Mtima wanga udzakondwera,
Mmene mundilandiranso.

Exit mobile version