Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 346 PEMPHERO ndiko kufuna,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 346 PEMPHERO ndiko kufuna,

 

PEMPHERO ndiko kufuna,
Kulakalakatu;
Ndi monga moto liyaka
Mumtima wa munthu.

Pemphero ndiko kulira,
Ngakhale misozi,
Kupenyetsetsa Kumwamba,
Mulungu mpafupi.

Pemphero ndiko kufuna
Kwa mwana wamng’ono;
Ndiponso mawu amphamvu
A munthu wamvanu.

Pemphero ndiwo mweyawo
Apuma akristu;
Ndi mapemphero tiloŵa
Dziko la imfalo.

Mutiphunzitse, Mbuyathu,
Kupempha kotero,
Kuyandikira kwa Mlungu
Ndi mtima wabwino.

Exit mobile version