Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 334 KULI dziko labwino M’mwamba,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 334 KULI dziko labwino M’mwamba,

 

KULI dziko labwino M’mwamba,
Lakuwala koposa dzuwa;
Yesu watikonzera malo,
Pokhalira ife komweko.

Bwinoli tipita,
Tikomana mwa dziko lija;
Bwinoli tipita,
Tikomana mwa dziko lija.

Tidzayimba komweko nyimbo,
Za abwino omvera Yesu;
Sitidzamva chisoni ife,
Tidzakondwa masiku onse.

Tidzatama Atate wathu,
Kuti Iye ‘napatsa Yesu;
Kuchotsera zochimwa zonse,
Ndikutidalitsatu ife.

Exit mobile version