Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 316 NDAMVATU kuti tifika komweko

Chichewa Christian Hymns

Hymn 316 NDAMVATU kuti tifika komweko

 

NDAMVATU kuti tifika komweko
Kuli Ambuye, Mtetezi wathuyo.
Ine, pakutha zobvuta zathuzo
Iye tidzamwona maso ndi maso.

Ndi Mbuyeyo tikhalamo,
Kupenyanso wokondatu;
Tidzakondwera, E, nthaŵi zonsezo
Ndicho chimwemwe ndi ulemutu.

Kaamba chisomo cha Mbuyathu uyu,
Malo okoma tipeza m’Mwambamo;
Kumva mtetezi amene ndi Yesu,
Ndicho chimwemwe ndi chachikulutu.

Onse aliko takonda kalelo,
Kale napita kwa Yesu Mbuyawo;
Koma kumwona Mtetezi wathuyo
Ndicho chimwemwe choposa, nchathucho.

Exit mobile version