Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 299 TIYENI, Akristu inu,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 299 TIYENI, Akristu inu,

 

TIYENI, Akristu inu,
Mumenyane nkhondo iyi,
Mukafoka nonse, koma
Yesu akulimbitsani.

Muyendanso kunka komwe,
Mugonjetse mdani wanu;
Musafoke, musaleme,
Musagone konse inu.

Musagonje, anthu inu,
Mtamiretu Yekha Mbuye;
Ipambana mphamvu yake,
Ya Mtsogoli wanu yemwe.

Mtima wanu wonse ndithu
Udzakhala ndi chimwemwe.
Zida zanu mbvale bwino
Zakudzera m’Mwamba momwe.

Limbikani inu nonse,
Msangalalo ngwanu nokha;
Musaope kanthu kena
Mumtamire Mbuye Yekha.

Tiyeni ku nkhondo iyi,
Mugonjetse zonse konko;
Muingitse mdani uja,
Muyendetse m’njira momwemo.

Exit mobile version