Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 298 IFE tazingidwa ndi zinthu zoopsa,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 298 IFE tazingidwa ndi zinthu zoopsa,

 

IFE tazingidwa ndi zinthu zoopsa,
Zachisautso chomwechili nkudza;
Cha nambala ya a sikisi atatu;
Kodi tidzapiliradi?

Kodi inu mayi mudzapiliradi
Kuyenda inu wausiwa.
Kodi inu bambo mudzapiliradi
Panthawi ya masautsowo?

Zizindikirozo zili kuwoneka,
Kutitu nkhondoyo yayandikadi;
Tisakhaletu odabwitsika konse,
Tilimbike kupemphera.

Tidzawona ena a ifetu zedi,
Tili kudindidwa pamphumi pathu;
Tidziwetu kuti sitinalembedwe,
Mayina m’buku mulibe.

Exit mobile version