Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 287 POKONDWA ndi poona vuto

Chichewa Christian Hymns

Hymn 287 POKONDWA ndi poona vuto

 

POKONDWA ndi poona vuto
Ndi tsoka pena mwayi,
Ndikumbukira, ndiimbira
Mulungu wangayo.

Kwezani nane Ambuyathu,
Timlemekeze yekha;
Popsinja mtima ndinamtchula,
Nandithangata ’ne

Angelo amazinga nyumba
Za anthu olungama;
Mulungu ateteza omwe
Amkhulupirira.

Laŵani chikondano chake;
Mudzadziŵitsa msanga
Kudala kwawo kwa anake
Omkonda Mbuyeyo.

Opani iye, nimuleke
Kuopa kanthu kena;
Mumtumikire mokondwera,
Akusungani ’nu.

Mulungu wathu Mmodzi yekha
Atate, Mwana, Mzimu,
Akhale ndi ulemerero
Wachikhalirewo!

Exit mobile version