Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 273 USAFUNE chuma chokha,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 273 USAFUNE chuma chokha,

 

USAFUNE chuma chokha,
Pena masewero okha;
Koma za Mulungu zokha,
Zipambana zinazo.

Ukafuna kulemera,
Pempha chuma chosathera;
Ndiwo mtima wakuyera,
Ndi wokonda Yesuyo.

Zosawutsa uvomere,
Ndipo Yesu chaulere;
Chikondano ndi mtendere,
Alowetsa m’mtimamo.

Zonse umazinyadira,
Udzaleka kusilira;
Uli nazo zokwanira,
Pakupeza Yesuyo.

Mbiri yake ubukitse,
Anthu onse nuphunzitse;
Kwa Mulungu nufikitse,
Osokera onsewo.

Yesu sakusiya konse,
Mphamvu, nzeru, chuma chonse;
Akupatsa nsiku zonse,
Tsata Yesu yekhayo.

Exit mobile version