Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 257 NJIRA yanga sindiziŵa,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 257 NJIRA yanga sindiziŵa,

 

NJIRA yanga sindiziŵa,
’Tate muikonza;
Komatu muzindikira
Kuti mundikonda.

M’mene mantha andigwira,
Andidetsa m’mtima,
Mbuye, ndithaŵire kwanu
Poti mundikonda.

Sindidziŵatu zamaŵa,
Koma sindiopa;
Ndidzakhulupira Inu
Kuti mundikonda.

Inde wakukonda ndinu;
Mawuwo oona
Andidzaza ndi chimwemwe:
Mlungu andikonda.

Exit mobile version