Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 216 NDISAUKA, ndinachimwa,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 216 NDISAUKA, ndinachimwa,

 

NDISAUKA, ndinachimwa,
Koma Inu m’nandifera;
Ndimo ndamva mund’itana,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Ndisauka, ndimasowa,
Mphamvu yakuyera m’mtima;
Mwazi wanu wanditsuka,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Ndisauka, sindikhoza,
Kuiletsa nkhondo m’ mtima;
Ndi chisoni, mantha nkhawa,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Ndisauka, sindiona,
Ndingodwala, ndilefuka;
Zonse ndizitaya kwa ‘Nu,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Inde, Yesu, mulandira,
Muchiritsa, m’ pulumutsa;
Mawu anu ndivomera,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Inde, Yesu, mundikonda,
Zonse zina ndazitaya;
Tsono kukhala wanu,
Mwana Mlungu ndingobwera.

Exit mobile version