Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 215 TATE ndili mwana wanu,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 215 TATE ndili mwana wanu,

 

TATE ndili mwana wanu,
Nkana ndinachimwa,
Ndingolirira kwa Inu;
Khululukireni.

Machimo anga ngambiri
Osaŵerengeka,
Ndingoyang’ana kwa Inu;
Khululukireni.

Ndinachimwa poganiza
Ndi polankhulanso,
M’ntchito zanga ndachimwanso;
Khululukireni.

Ndinachita mphulupulu,
Ndinakunyozani,
M’ntchito zanga ndalephera;
Khululukireni.

Zonse ndinakonda kale
Ndi zopanda pake,
Sindinakhuta nazotu;
Khululukireni.

Exit mobile version