Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 213 INE ndili ndi manyazi

Chichewa Christian Hymns

Hymn 213 INE ndili ndi manyazi

 

INE ndili ndi manyazi
Kuti kale lomwelo
Ndinanyoza kudza komwe
Kwa Mtetezi wanga Yesu,
Ndati, Sindimfuna `yi.

Koma Iye wandipeza;
Ndamuona m`mtandamo,
Mwa kufera ine momwe;
Ndipo ndati m`mtima mwanga:
Mbuye, ndikufunani.

Nsiku zonse kwanja kwake
Kunandithandizatu,
Kunandichiritsa mtima;
Ndipo ndati: Mpulumutsi,
Ndinu Mbuye wangatu.

Sindifuna Mbuye wina,
Koma Yesu yekhayo;
Ine ndili munthu wake,
Iye anandigonjetsa
Ndi kukonda kwakeko.

Exit mobile version