Chichewa Christian Hymns
Hymn 199 NDINASOKERA kutali,
NDINASOKERA kutali,
Ndinadya ndi nguluwe,
Ndinakhala mu zoipa,
Chifukwa ndinachimwa.
Mmene ndafika
kwa ‘tate,
Nandikonzeratu phwando;
“Tidye tisekere naye,
Mwanayu anasowa.”
Koma mkulu wanga ndiye,
Sanandirandiretu;
Sanafune tate wanga,
Andikhululukire.
Ambuye amayitana,
Anthu onse ochimwa;
Kuti adzetu kwa Iye,
Kumene kuli moyo.
