Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 191 AMBIRI tikondwera mwa Yesu,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 191 AMBIRI tikondwera mwa Yesu,

 

AMBIRI tikondwera mwa Yesu,
Nanga inu? Nanga inu?
Tapeza chipulumutso ndithu;
Nanga inu?

Masiku onse timakondwera
Pakumva Mawu ake a Yesu;
Wolalikira tidzamumvera;
Nanga inu?

Ife tiyembekezera YESU,
Nanga inu? Nanga inu?
Chimwemwecho chilimumtimamu;
Nanga inu?

Titasokera tinabwerera,
Nanga inu? Nanga inu?
Tidziŵa kuti ndiwo uchimo;
Nanga inu?

Tinachoka munjira ya imfa,
Nanga inu? Nanga inu?
Takopeka ndi Mawu a Yesu;
Nanga inu?

Exit mobile version