Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 185 NDINE Mbusayo wabwino,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 185 NDINE Mbusayo wabwino,

 

NDINE Mbusayo wabwino,
Ndinafera nkhosazo;
Yotayika ndayifuna,
Mpaka ndataya moyo

Mbulu wanding’amba m’nthiti,
Wanding’ambanso m’manja,
Wanding’ambira zovala,
Ndatsala wawumphawi.

Nkhosa zanga
Zimandimva,
Ndikaziyitanazo;
Ndimazipatsa moyowo,
Atate nazisunga.

Atate wondipatsazo,
Ali nayo mphamvutu,
Kuzidyetsa, kuzisunga,
Palibe wolandazo.

Musawone zovalazo,
Mkati ali fisiyo;
Musanyengedwe anthuni,
Ine ndine Mbusayo.

Tamverani anthu inu,
Ine ndine Mbusayo,
Ndine njira, ndine khomo,
Thawani mimbuluyo.

Exit mobile version