Chichewa Christian Hymns
Hymn 162 PENYETSETSA Yesu,
PENYETSETSA Yesu,
Mtima wosauka; Anafera iwe,
Idza, nupumule.
Iye anachotsa
Nsoni ndi zoipa;
Penyetsetsa Yesu,
Ndi kukhulupira.
Penyetsetsa Yesu
Likatentha dzuŵa;
Yachuluka ntchito,
Mphamvu idzakula.
Akonzera kwawo
Nyumba zokhalamo;
Penyetsetsa Yesu,
Mtsatetu tsopano.
Penyetsetsa Yesu
Pogwirana nawo;
Nkhondo ikabvuta
Tamva Mbuye wako.
Achuluka’dani,
Iwe ungofoka;
Penyetsetsa Yesu,
Mantha adzachoka.
Ndipo pakuloŵa
M’dziko la Kumwamba,
Udzapeza komwe
Onse adzatama.
Mwa zoŵala zija
Za Kumwamba kwawo,
Udzapenya maso
Yesu Mbuye wako.
