Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 161 LERO lino mbale wanga,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 161 LERO lino mbale wanga,

 

LERO lino mbale wanga,
Ndilo tsiku lakukoma;
Talandira Mpulumutsi,
Mmene ali kuyitana.

Lero lino mbale wanga,
Usazengereze ayi;
Ngati ulandira Yesu,
Lero, udzachita mwayi.

Lero lino ndi labwino,
Moyo wako uli nawo;
Pena mawa umwalira,
Udzatani mlandu wako?

Lero lino mbale wanga,
Lapa mtima, lapa tchimo;
Yesu adzakulandira,
Ukam’pempha lero lino.

Ndiwe mlendo lero lino,
Myera ndikupempha iwe:
Yesu Mwana wa Mulungu,
Akufuna ndithu iwe.

Inde, lero lino Yesu,
Ayitana inu nonse;
Landirani Mpulumutsi,
Musazengereze konse.

Exit mobile version