Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 14 MTIMA wanga uyamike,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 14 MTIMA wanga uyamike,

 

MTIMA wanga uyamike,
Mfumu ya Kumwambako,
Anandiwombola ine;
Nanditsuka m’mtimamo.

Ife tonse, ife tonse,
Tiyamike Mlunguyo.

Tiyamike Mulungu wathu,
Kaamba ka chifundocho;
Nthaŵi zonse sasinthika,
Mlungu wathu yemweyo.

Nthaŵi zonse monga Tate,
Atisamaliratu;
Atisunga m’manja mwake,
Atipulumutsatu.

Anthu a mitundu yonse,
Ndiponso a Kumwamba;
Yamikani Mungu wathu,
Ndiye wakukomatu.

Anthu onse, anthu onse,
Yamikani Mlunguyo.

Exit mobile version