Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 76 E, MOYO wanga’we

Chichewa Christian Hymns

Hymn 76 E, MOYO wanga’we

 

E, MOYO wanga’we
Utsitsimuketu;
Ambuye Yesuyo
Akhala m’Mwambamo.
Pampandopo
Akhalabe, natchula dzina langali.

Kwa Mlungu m’Mwambamo
Amapempherako;
Chikondi chakenso
Chikhala chosatha;
Ndi mwaziwo
Akhalatu Wansembe wanga Yesuyo.

Mabala ajawo
A m’thupi mwakemo
Amukumbutsanso
Za ine pansipa;
Zoipazo
Achotsadi kotero sindingafe’yi

Mulungu ali wokhulula mtimatu,
Ndilibe mantha’yi,
Andisungiradi;
Ndibwera kwa
Atatewo, titayanjana leroli.

Exit mobile version