Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 444 YEMWE afesa nalira,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 444 YEMWE afesa nalira,

 

YEMWE afesa nalira,
M’chikonditu mbewuzo;
Osatopa, osagona,
Yesu amadalitsa.

Ona mmera wakukondwa,
Dzinthu zonse dzachanso;
Ona m’minda mwayeratu,
Kukunkha kwayandika.

Fesa mbewu usatope,
Usaope konsetu;
Nkana utapeza vuto,
Udzatuta mokondwa.

Mvula idzathilirapo,
Dzuwa lidzawalira;
Ndi zipatso zidzabala,
Mphamvu ya Mulunguyo.

Exit mobile version