Chichewa Christian Hymns
Hymn 425 AKRISTU ndi abale, tiziyenderana tonse,
AKRISTU ndi abale, tiziyenderana tonse,
Mulungu mmodzi tili naye, ndi Ambuye yemwe,
Chitsime chomwe, njira yomwe yokhulupirira;
Tiyeni tonse, m’Mpingo ’modzi tiziyenderana.
Atate yemwe anatuma,
Mpulumutsi mmodzi
Kudzatifera kuti atiyanjanitse tonse,
Ndi Mzimu yemwe ayeretsa akumvera onse;
Tiyeni tonse, m’Mpingo ’modzi tiziyenderana.
Anatipatsa Mawu omwe olimbitsa mtima;
Kumwamba komwe tinka ndi kulonda njira yomwe.
Tibalalikiranji ife akutsata Yesu?
Tiyeni tonse, mMpingo ’modzi tiziyenderana.
Satana apambana tikayamba kusiyana;
Tikayanjana, yemwe adzagonja ndi kuthaŵa;
Mbuyathu adzamthyola konse ndi kumlamulira.
Tiyeni tonse, m’Mpingo ’modzi tiziyenderana.
Tiphatikane tonsefe okonda Yesu Kristu;
Tisalekane pakugwira ntchito za Mbuyathu;
Tilimbitsane pakuyenda m’njira yonka kwathu.
Tiyeni tonse, m’Mpingo ’modzi tiziyenderana.
