Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 386 MONGATU mawu anuwo,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 386 MONGATU mawu anuwo,

 

MONGATU mawu anuwo,
Ndi Mtima chete phee,
Mbuyanga kufa kwanuko
Ndikumbukire ’ne.

Chakudya chakumwambachi
Ndi thupi lanudi;
Chikho cha chipanganochi
Ncha mwazi wanuwo.

Getsemane ndionako
Ndi nkhope yanu dwii,
Thukuta la pamphumilo
La myazi yanuyi.

Ndi mtanda uli m’maso mbuu,
Ndiona m’menemo,
A Yesu kufa kwanuko,
Kuthetsa imfazo.

Pamene padzakhalapo
Milomo yanga phee,
Mukadza ndi Ufumunso,
Mukumbukire ’ne.

Exit mobile version