Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 382 M’wabatize anzathuwa,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 382 M’wabatize anzathuwa,

 

M’wabatize anzathuwa,
Ndi Mzimu wanu Woyera;
Chikhale chizindikiro,
Cha chikondi chanu chija.

Batizeni, batizeni!
Batizeni, batizeni!
Ndi Mzimu wanu Woyera!

Pobatizidwa ndi madzi,
M’wabatizenso ndi mwazi;
Kuwayeretsa mitima,
Ndi mwazi wanu womwewo.

Tifike tonse kumtsinje,
Wamwazi wa Mbuye Yesu;
Tiyeretsedwe tonsefe,
Ndi mwazi wanu womwewo.

Tibatizeni tonsefe,
Ndi Mzimu wanu Woyera;
Chikhale chizindikiro,
Cha chikondi chanu chija.

Exit mobile version