Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 37 YESU analikhanda

Chichewa Christian Hymns

Hymn 37 YESU analikhanda

 

YESU analikhanda
M’Betlehemumo;
M’ngelo anasimba za
Kubadwa kwake.

Kubadwa kwa Yesu
M’Betlehemumo;
Khandalo linagona
M’khola la ng’ombe.

Mngelo anatumidwa
Kuŵasimbira
Abusa a nkhosa za
Kubadwa kwake.

Anapita nasiya
Nkhosa zawozo;
Anapita kumudzi
Kukamlambira.

“Tadodoma, abusa,
Kwachitikanji?
Mwazisiyira yani
Nkhosa zanuzo?”

“Posunga nkhosa ife
Kubusa kwathu
Mngelo anasimba za
Kubadwa kwake.”

Exit mobile version