Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 363 ATATE ndiyamika,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 363 ATATE ndiyamika,

 

ATATE ndiyamika,
Mwandisamalira leroli;
Mulungu wandikonda,
Mndisungenso m’mdima muno bii.

Mundikumbutse, ndikapanda tulo,
Za Kumwambako;
Zoganizira, zoipitsa,
M’mtima muchotseremo.

Zochimwa za usana uno
Mndikhululukire ’ne;
Mtendere wanu muloŵetse;
M’mtima ndikagone phee!

Mundilimbitse ndikayese,
Manda ngati mphasayi,
Nditagonamo ndikadzuke,
Tsiku lomalizalo.

Tiyamike Mlungu wotipatsa,
Zachifundozi;
Amyamikire onse,
A Kumwamba ndi apansipa.

Exit mobile version