Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 359 TADZUKA mzimu wanga ‘we,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 359 TADZUKA mzimu wanga ‘we,

 

TADZUKA mzimu wanga ‘we,
Ugwire ntchito zakozi;
Kukondwa ukutengedi,
Pemphero ulikwezedi.

Pemphero, pemphero,
Pemphero ulikwezedi;
Pemphero, pemphero,
Pemphero ulikwezedi.

E, nthawi ya m’mamaŵayi,
Um’tamandire Mbuyeyo;
Nuyese lero ngatitu,
Tsiku lakumalizalo.

Munkhani zako zonsetu,
Unene molungamadi;
Nudziwe kuti Mbuyako,
Adziwa zachinsinsizi.

Patsikuli, Mbuyanga ‘Nu.
Munditsogoze m’njiramo;
Ulemelero wanuwo,
Undilimbitse monsetu.

Tim’lemekeze Mlunguyu,
Wamadalitso onsewo;
Tim’lemekeze tonsefe,
Atate, Mwana, Mzimunso.

Exit mobile version