Chichewa Christian Hymns
Hymn 325 KODI uli ndi chisoni
KODI uli ndi chisoni
Choliritsa mtima wako?
Kweza maso, ndi Atate
Akumvetsa zonsezi.
Kodi umadandaula;
“Mbale wanga waferanji?”
Kumbukira Wakumtenga
Saphophonya konse ’yi.
Mbale wako unamkonda,
Koma Yesu amkondetsa;
Anamfuna nagomtenga;
Usammane Yesu’yi
Pakutsazikana nanu
Ndi potseka maso ake,
Imfa, bii! Anangogona
Koma adzadzukanso.
Usalire; Mpulumutsi
Analaŵa imfa Yekha;
Imfa yomwe nagonjetsa
Potuluka m’mandamo.
Chikondano sichifera;
Mbale wako udzamwona
Kwathu komwe; zipirira
Mpaka ukafikako.
Leroli chisoni chokha,
Tsiku lija kungokondwa;
Kweza maso osalira,
Yesu akukondadi.
