Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 321 PAKUONA imfayo

Chichewa Christian Hymns

Hymn 321 PAKUONA imfayo

 

PAKUONA imfayo
Chisonicho chikula
Ndilira misozi.

Ndilira, ndilira,
Ndilira Mbuye Yesu wangadi.
Ndaimba ndi kulira ndi kusisima,
Ndaimba ndi kulira ndi kusisima,
Ha! Ha! Aleluya!
Ha! Ha! Aleluya!
Mwasiyiranji Ambuye Yesu?

Ndinasiya amayi,
Ndinasiya atate,
Abale komweko.

Kazembe wanga m’matenda,
Ndili m’manja mwa Mbuye.
Abale tsalani.

Zoipa zakanikadi,
Sizikhoza kuchotseka,
Ndilira misozi.

Angelo aitana,
Aitana Kumwambako,
Tiyeni, tikwere!

Munafera pa mtanda
Chifukwa cha inedi,
Si cha wina ayi.

Exit mobile version