Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 311 VALANI zida tizinka kwathuko,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 311 VALANI zida tizinka kwathuko,

 

VALANI zida tizinka kwathuko,
Tikayimbire Mulungu wa moyo;
Matupi athu adzasandulika,
Popita kwathuko.

Kwathu Kumwamba uko,
Moyo uliko uko;
Zowawa zonse uko kulibe,
Tidzayimbira pamodzi ndi Angelo,
Popita kwathuko.

Wotsogolera ndi Mbuye Yesuyo,
Paulendotu wopita kwathuko;
Tidzanyamula mbendera
Ya M’mwamba,
Popita kwathuko.

Pamene tonse tifika kwathuko,
Adzatipatsa korona wa moyo;
Tikayimbira Mulungu wa M’mwamba,
Pofika kwathuko.

Exit mobile version