Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 225 NDIDZAIMBA za Mulungu,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 225 NDIDZAIMBA za Mulungu,

 

NDIDZAIMBA za Mulungu,
Zakukonda kwakeko;
Anatuma Mwana wake,
Kundifera kalero.

Inde ndidzayimba nyimbo,
Za kukonda kwakeko;
Ndidzayimba ndi angelo,
Akukhala M’mwambamo.

Ndinachita mphulupulu,
Wayiwala zonsezo!
Ndinakhala ndi zoipa,
Wazichotsa zonsezo!

Wandipatsa moyo wake,
Moyo wakuyera mbuu!
Ine ndili mwana wake,
Wandilera inetu.

Ndiyamika Mbuye wanga,
Ndidzam’lemekezabe;
Ndipititsa mbiri yake,
Yakukonda kwakeko.

Exit mobile version