Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 201 NDILINKUDZA kwa Ambuye,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 201 NDILINKUDZA kwa Ambuye,

 

NDILINKUDZA kwa Ambuye,
Ndisauka, ndinachimwa;
Zanga zonse ndizisiya,
Kudzapeza moyo wina.

Yesu ndikhulupirira,
Munafera ine ndemwe;
Mwaumphawi ndipemphera,
Mundipulumutse tere.

Kale ndinalira Inu,
Kale lomwe ndangochimwa;
Mundiitana: “Idza kuno,
Kuti n’kuchotsere tchimo.”

Yesu, n’kupatsani zonse,
Zili zanu zokhazokha;
Thupi lonse mtima womwe,
Mwini wake ndinu nokha.

E, ndikukhulupi’rani,
Ndauwona mwazi wanu;
Tere ndikugwadirani,
Tere ndapachikwa nanu.

Wadza Yesu, wandidzoza,
Ndakonzeka mwa Iyeyu;
Ndine wake, takondana,
Ndiyamika Mbuye Yesu.

Exit mobile version