Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 188 MPULUMUTSI Wokondedwa,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 188 MPULUMUTSI Wokondedwa,

 

MPULUMUTSI Wokondedwa,
Mwandipulumutsa ine;
Ndine wanu, wanu nokha,
Wotsukidwa m’mwaziwo.

Aleluya, Aleluya,
Mwanawankhosa ndinutu:
Mwazi wanu wanditsuka,
Aleluya kwa Yesu.

Mtima wanga wabvutika,
Zaka zonse ndingochimwa;
Tsono sindikangalika,
Ndingopuma mwa Yesu.

Mwandipatulira ine,
Kwa Inu ndidzipereka,
M’moyo, m’imfa mboni yanu
Ya chipulumutsocho.

Aleluya, mwandigula,
Ndipo mudzandisungabe;
Mwazi wanu ndi wamphamvu
Kuyeretsa konseko.

Exit mobile version