Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 179 TUMPHATUMPHA moyo wanga,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 179 TUMPHATUMPHA moyo wanga,

 

TUMPHATUMPHA moyo wanga,
Sangalala ndi Mtetezi;
Kuwombola kwa Yehova
Kwatuluka m’dziko lako.

Mulungu wakwezekatu,
Mpulumutsi m’dziko lako,
Wakwezekatu Chitetezo.
Wabvundikira iwedi
Mzimu wanga’we wafunda,
Lulutiratu moyo wanga.

Bvinabvina moyo wanga,
Lulutira mtima wanga;
Wa mawuwo a Yehova
Watuluka m’dziko lako.

Imbirira moyo wanga,
Mtendere wako wafika;
Mbendera ya Chitetezo
Waikwezetsa ndi Yesu.

Ukondwere moyo wanga,
Kuunika kuoneka,
Ndi mdimawo uthaŵatu;
Lulutira moyo wanga.

Usekere moyo wanga,
Ndi Yehova akufuna;
Wakwezatu mbenderayo
Ya Chitetezo, sekera.

Exit mobile version