Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 17 MULUNGU ndiye Mbusa wanga,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 17 MULUNGU ndiye Mbusa wanga,

 

MULUNGU ndiye Mbusa wanga,
Sindisoŵa konse;
Amandiŵeta nandidyetsa,
Nandipatsa zonse.

(Ndiye Mbusa wanga,
Ndiye Mbusa wanga!
Mulungu ndiye Mbusa wanga,
Sindisoŵa konse)

M’mitsinje yamtendere mtima,
Wanga aumwetsa;
Mapazi omwe m’njira,
Yolungama nayendetsa.

Za mdima, imfa, nkhondo ndi zoipa sindiopa;
Ndikakhumudwa ndi kutopa,
Andipulumutsa.

Podwala ine, povutidwa,
Andisamalira;
Pondisautsa ’dani anga
Nandithangatira.

Chisomo ndi zokoma zake,
Sizileka konse;
Ndi m’nyumba ya Mulungu,
Ndidzakhala nsiku zonse.

Exit mobile version