Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 167 KODI mwalandira Yesu?

Chichewa Christian Hymns

Hymn 167 KODI mwalandira Yesu?

 

KODI mwalandira Yesu?
Iye anakuferani.
Afunitsa inu nonse;
Kodi mumufunanso?

Kodi mufunatu Yesu?
Bvomerani msangatu:
“Inde Yesu ndifunadi,
Ndinu Mbuye wangatu.”

Nthaŵi zonse mufunabe
Zinthuzo za pansi pano;
Koma munyozabe Yesu
Wopachikidwa kalelo.

Yesu akuitanani
Kwanja kwake kwakukulu;
‘Mvani mawu ake lero,
Musachite nthantha’yi

Imfa idzafika msanga;
Ndipo mdzaikidwa m’manda;
Nthaŵi yomwe simudzamva
Kutitana kwakeko.

Exit mobile version