Chichewa Christian Hymns
Hymn 153 NDAKUMANA ndi bwenzi lokomalo,
NDAKUMANA ndi bwenzi lokomalo,
Ndiye Yesu mtetezi wanga;
Ndayang’ana, palibe wina padziko.
M’mtima mwanga mualowa chisangalalo,
Popeza ndawomboledwa;
(Chinanso) ndalandira
Mzimu Woyera (zedi)
Moyo wanga wawomboledwa
Ndasamba m’mwazi wa chitsime chake,
Cha Ambuye mtetezi wanga;
Ndayang’ana, palibe wina padziko.
Ndayera ndi mwazi wa Ambuyeyo,
Ndine wake wa Ambuyewo;
Ndayang’ana, palibe wina padziko.
