Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 140 NDINAMIRA m’machimo, wosaonekanso,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 140 NDINAMIRA m’machimo, wosaonekanso,

 

NDINAMIRA m’machimo, wosaonekanso,
Ndinamira ndithudi wosatulukanso;
Koma Yesu adamva
Kulira kwangako,
Nandipulumutsa kumachimowo.

Nandikweza,
Nandikweza,
Pomira m’thopemo,
Nandikweza;
Nandikweza,
Nandikweza,
Pomira m’thopemo,
Nandikweza.

Mtima wanga ndipatsa ndidzam’kangamira,
Ndidzakhala mwa Iye ndikumuyimbira;
Mtima wanga uyimba
Za chikondi chake,
Tsono ndidzatumikira Yesuyo.

Ovutika penyani,
Yesu wolanditsa;
Adzakutulutsani
M’mafunde owopsa;
Ndiye Mwini nyanjayo, mafunde amvera;
Akhozadi kukupulumutsani.

Exit mobile version