Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 129 WODALA ndiye munthuyo,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 129 WODALA ndiye munthuyo,

 

WODALA ndiye munthuyo,
Wosayenda moyipa;
Wosayimilira m’njira,
Ya anthu ochimwawo,
Ya anthu ochimwawo.

M’chilamulo cha Yehova,
Amakondwereramo;
Ndipo amalingilira,
Usana ndi usiku,
Usana ndi usiku.

Akunga mtengo wooka,
Pamitsinje yamadzi;
Chipatso chake chopatsa,
Panyengo yake yonse,
Panyengo yake yonse.

Kapena sakhala pansi,
Pabwalo la onyoza;
Zonse azichita iye,
Amapindula nazo,
Amapindula nazo.

Oyipa akunga mungu,
Wouluka ndi mphepo;
Mumsonkhano olungama,
Sadzaimilirako,
Sadzaimilirako.

Mayendedwe olungama,
Yehova awadziwa;
Koma oyipa onsewo,
Adzataika ndithu,
Adzataika ndithu.

Exit mobile version